Wolemba ntchito ku Vatican News
Mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Francisco watumiza uthenga kwa omwe atenga nawo mbali pa mwambo wa 102 wa masiku a Catholic Days (Katholikentag) otsegulira Lachitatu madzulo mu mzinda wa Stuttgart ku Germany ndikupitilizabe mpaka Lamlungu.
Papa anapereka moni wake wachikondi m’masiku achikondwerero ameneŵa pamene amasonkhana “kulemekeza Mulungu ndi kuchitira umboni pamodzi za chisangalalo cha Uthenga Wabwino.”
"Kugawana moyo"
Ponena za mawu a Katholikentag, Papa ananena kuti Mulungu “anauzira mpweya wake wa moyo mwa anthu,” ndipo mwa Yesu “gawo la moyo” limeneli la Mulungu likufika pa “nsonga yosayerekezeka” pamene “akugawana nawo moyo wathu wapadziko lapansi kuti uthandize anthu kukhala ndi moyo wosatha. kuti titenge nawo mbali mu moyo wake waumulungu.”
Timayitanidwanso kutsatira chitsanzo cha Yesu posamalira osauka ndi ovutika, monga momwe ife lerolino tili pafupi ndi anthu a ku Ukraine ndi onse omwe akuopsezedwa ndi ziwawa, Papa adanena, kutipempha tonsefe kupempha mtendere wa Mulungu pa anthu onse.
Kupatulira miyoyo yathu kwa Mulungu ndi anzathu
Papa wati tikhoza kupereka mphatso ya moyo wathu kwa Mulungu ndi anzathu munjira zosiyanasiyana, kaya amayi ndi abambo odzipereka akulera ana awo kapena opereka nthawi yawo mu mapemphero a tchalitchi ndi ntchito zachifundo. Papa anatsindika kuti "palibe amene apulumutsidwa yekha" komanso "tonse tikukhala m'ngalawa imodzi" zomwe zimapangitsa kuti tikhale ozindikira kuti tonsefe ndife "ana a Atate mmodzi, abale ndi alongo" ndipo tiyenera kukhala mu mgwirizano wina ndi mzake.
Chitsanzo chowala cha St. Martin
Papa analozera kwa Martin Woyera, woyang’anira dayosizi ya Rottenburg-Stuttgart, monga “chitsanzo chowala” choti atsatire, amene anagawana chofunda chake ndi munthu wosauka amene akuvutika ndi kuzizira ndi kumuchitira ulemu ndi chisamaliro, osati kungopereka chithandizo.
Kupereka ndi kulandira mphatso
Pomaliza, Papa anaona kuti ngakhale osauka ali ndi chinachake chimene angapereke kwa ena, ndipo ngakhale olemera kwambiri akhoza kusowa chinachake ndikusowa mphatso za anthu ena. Iye anaona kuti nthawi zina zingativute kulandila mphatso, cifukwa zimafuna kuvomeleza kuti ndife opanda ungwilo ndi zosoŵa zathu, ngakhale titadziona kuti ndife okwanila. Iye ananena kuti tiyenera kupemphera kwa Mulungu kuti atipatse “kudzichepetsa n’kulandira zinthu kuchokera kwa ena.”
Pomaliza, Papa analozera kwa Namwali Wodalitsika Mariya ndi chitsanzo cha “kudzichepetsa kumeneku kwa Mulungu,” chimene chiyenera kusonyeza maganizo athu. “Iye anachonderera ndi kuyembekezera Mzimu Woyera pakati pa atumwi, ndipo mpaka lero, ndi ife ndi pambali pathu, iye akupempha mphatso iyi pakati pa mphatso.”